Zechariah 9

Chiweruzo pa Adani a Israeli

Ulosi

1Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki
ndi mzinda wa Damasiko
pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli
ali pa Yehova—
2ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli,
komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
3Ndipo Turo anadzimangira linga;
wadziwunjikira siliva ngati fumbi,
ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
4Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho
ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja,
ndipo adzapserera ndi moto.
5Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha;
Gaza adzanjenjemera ndi ululu,
chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu.
Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa
ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
6Mu Asidodi mudzakhala mlendo,
ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
7Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo,
chakudya choletsedwa mʼmano mwawo.
Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu,
adzasanduka atsogoleri mu Yuda,
ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
8Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga
ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza.
Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga,
pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.

Kubwera kwa Mfumu ya Ziyoni

9Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni!
Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe,
yolungama ndi yogonjetsa adani,
yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu,
pa mwana wamphongo wa bulu.
10Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu
ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu,
ndipo uta wankhondo udzathyoka.
Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu.
Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina,
ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
11Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine,
ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
12Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo;
ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
13Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga,
ndipo Efereimu ndiye muvi wake.
Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni,
kulimbana ndi ana ako iwe Grisi,
ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.

Kuoneka kwa Yehova

14Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake;
mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani.
Ambuye Yehova adzaliza lipenga;
ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
15ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza.
Iwo adzawononga
ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni.
Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo;
magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi
pa ngodya za guwa lansembe.
16Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa
pakuti anthu ake ali ngati nkhosa.
Adzanyezimira mʼdziko lake
ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
17Taonani chikoka ndi kukongola kwawo!
Tirigu adzasangalatsa anyamata,
ndi vinyo watsopano anamwali.
Copyright information for NyaCCL